Site icon 247MALAWI NEWS

Mumba alimbikitsa anthu aku Likoma ndi Chizumulu kukhala pambuyo pa Chakwera




Wolemba: Mtolankhani wathu


Wachiwiri kwa President Lazarus Chakwera pachisankho cha pa 16 September, a Vitumbiko Mumba alimbikitsa anthu apa zilumba za Likoma ndi Chizumulu kupitilira kukhala pambuyo pa President Chakwera pakuti ndiyekhayo yemwe ali ndi masomphenya wotukula zilumbazi.

A Mumba omwenso ndi nduna ya zamalonda ndi mafakitale apereka pempholi lachisanu pomwe anayenda ulendo wa pa madzi kukacheza ndi anthu apa zilumbazi.

A Mumba ati President Chakwera ndiwokonzeka kutukula maderawa komanso ntchito za maulendo apa nyanja zomwe maboma ena ammbuyomu samaziyikira pamtima.

Mumba



Pamenepa a Mumba ati anthu apa zilumbazi omwe analembetsa mkaundula wazisankho, akuyenera kuvotera a Chakwera lachiwiri sabata ya mawa ndipo kuti asapusitsike ndi atsogoleri ena adyera omwe akungofuna kuwagwiritsa ntchito kuti apeze mavoti

Pa ulendowu a Mumba anaperekezedwa ndi mkulu wa achinyamata mchipani cha MCP a Baba Steven Malondera ndi akuluakulu ena.

Chipani cholamula cha Malawi Congress ndichomwe chikuoneka kuti chiri ndi chikoka pa zilumbazi potengera unyinji wa anthu omwe wakhala ukusonkhana m’misonkhano yachipanichi.

Exit mobile version