Saturday, September 13, 2025
No menu items!
spot_img
HomePoliticsMumba alimbikitsa anthu aku Likoma ndi Chizumulu kukhala pambuyo pa Chakwera

Mumba alimbikitsa anthu aku Likoma ndi Chizumulu kukhala pambuyo pa Chakwera




Wolemba: Mtolankhani wathu


Wachiwiri kwa President Lazarus Chakwera pachisankho cha pa 16 September, a Vitumbiko Mumba alimbikitsa anthu apa zilumba za Likoma ndi Chizumulu kupitilira kukhala pambuyo pa President Chakwera pakuti ndiyekhayo yemwe ali ndi masomphenya wotukula zilumbazi.

A Mumba omwenso ndi nduna ya zamalonda ndi mafakitale apereka pempholi lachisanu pomwe anayenda ulendo wa pa madzi kukacheza ndi anthu apa zilumbazi.

A Mumba ati President Chakwera ndiwokonzeka kutukula maderawa komanso ntchito za maulendo apa nyanja zomwe maboma ena ammbuyomu samaziyikira pamtima.

Mumba



Pamenepa a Mumba ati anthu apa zilumbazi omwe analembetsa mkaundula wazisankho, akuyenera kuvotera a Chakwera lachiwiri sabata ya mawa ndipo kuti asapusitsike ndi atsogoleri ena adyera omwe akungofuna kuwagwiritsa ntchito kuti apeze mavoti

Pa ulendowu a Mumba anaperekezedwa ndi mkulu wa achinyamata mchipani cha MCP a Baba Steven Malondera ndi akuluakulu ena.

Chipani cholamula cha Malawi Congress ndichomwe chikuoneka kuti chiri ndi chikoka pa zilumbazi potengera unyinji wa anthu omwe wakhala ukusonkhana m’misonkhano yachipanichi.

RELATED ARTICLES
- Advertisment -
Google search engine

Most Popular

Recent Comments